Chichewa 2. Buku la ophunzira la Sitandade
 9789996044014

  • Author / Uploaded
  • coll.

Citation preview

Malawi Primary Education

Chichewa

T Y ED UC

AT I

O

LL RA

MO TI

ALI QU

FO

PRO

G

N

N

Buku la ophunzira la Sitandade

Adakonza ndi kusindikiza ndi a Malawi Institute of Education PO Box 50 Domasi Zomba Malawi Email: [email protected] Website: www.mie.edu.mw

© Malawi Institute of Education, 2017

Zonse za m’bukumu n’zosati munthu akopere mu njira ina iliyonse popanda chilolezo. N’zosatinso munthu achitire malonda mpang’ono pomwe. Komabe ngati munthu afuna kugwira ntchito ya zamaphunziro ndi bukuli, ayambe wapempha ndi kulandira chilolezo kuchokera kwa eni ake omwe adalisindikiza.

Kusindikiza koyamba 2017

ISBN 978-99960-44-014

Olemba Jeremiah Kamkuza

: D  epartment of Inspection and Advisory Services

Foster Gama

: Malawi Institute of Education

Frackson Manyamba

: Malawi Institute of Education

Lizinet Daka

: Department of Basic Education

Wisdom Nkhoma

: Domasi College of Education

Laston Mkhaya

: Montfort Special Needs College

Benjamin David

: Blantyre Teachers’ College

Irene Kameme

: Blantyre Teachers’ College

Rex Chasweka

: Blantyre Teachers’ College

Jordan Namondwe

: Chiradzulu Teachers’ College

Luke Njovuyalema

: Lilongwe Teachers’ College

Mordky Kapesa

: Lilongwe Teachers’ College

Esther Chenjezi Chirwa

: Lilongwe Teachers’ College

Mike Rambiki

: Lilongwe Teachers’ College

Elias Chilenje

: Phalombe Teachers’ College

Adriana Mpeketula Mafunga : Phalombe Teachers’ College Owen Kazembe

: Kasungu Teachers’ College

Nicholas Kalinde

: Machinga Teachers’ College

Samson Khondiwa

: Malawi Institute of Education

Rabson Madi

: DTED

Margaret Sapili Luhanga

: Mmanga Primary School

Ryphen Chibwana

: Mmanga Primary School

Kuthokoza A Unduna wa za Maphunziro, Sayansi ndi Luso pamodzi ndi a Malawi Institute of Education akuthokoza onse omwe adathandizapo mu njira zosiyanasiyana kuyambira polemba bukuli kufika polisindikiza. Iwowa akuthokozanso kwakukulu bungwe la United States Agency for International Development (USAID) ndi United Kingdom Aid (UKAID) pothandiza ndi ndalama komanso upangiri polemba, pounika ndi kusindikiza buku la ophunzirali mogwirizana ndi Mlingo wa Boma Wounikira Maphunziro M’sukulu (National Education Standards) komanso Ndondomeko ya Boma Yokhudza Kuwerenga M’sukulu (National Reading Strategy). A Unduna wa za Maphunziro, Sayansi ndi Luso pamodzi ndi a Malawi Institute of Education akuthokozanso anthu onse omwe adaunika bukuli ndi kupereka upangiri osiyanasiyana.

Okonza bukuli Akonzi

:  Max J Iphani, Peter Ngunga, Sylvester Ngoma ndi Ella Kulekana-Madambo

Ojambula Zithunzi

: Heath Kathewera, Isaiah Mphande, Richard Mwale, Henderson Mawera Raphael Mawera ndi Mphatso Phiri

Wotayipa

: Lucy Kalua-Chisambi ndi Raymond Tchuka

Woyala Mawu ndi Zithunzi : Sanderson Ndovi Mkonzi Wamkulu

: Max J Iphani

iv

Zamkatimu

Kuthokoza ............................................... iv

MUTU 1 Malonje akusukulu.................... 1

MUTU 2 nd ch....................................... 12 MUTU 3 dz ph....................................... 18 MUTU 4 mf m’b..................................... 25 MUTU 5 Kubwereza............................... 31 MUTU 6 mph nth.................................. 35 MUTU 7 tch mgw.................................. 44 MUTU 8 ng’w mch................................. 52 MUTU 9 khw phw.................................. 59 MUTU 10 Kubwereza............................... 67 MUTU 11 mg mm.................................... 71 MUTU 12 pw sh...................................... 78 MUTU 13 zw zy...................................... 85 MUTU 14 nkh ngw.................................. 92 MUTU 15 Kubwereza............................... 100 MUTU 16 mts.......................................... 104 MUTU 17 mbw......................................... 108 MUTU 18 ndw......................................... 112

MUTU 19 thw.......................................... 116 MUTU 20 Kubwereza............................... 119 MUTU 21 thy........................................... 122 MUTU 22 tsw.......................................... 126 MUTU 23 msw......................................... 130 MUTU 24 nsw.......................................... 133 MUTU 25 Kubwereza............................... 137 MUTU 26 mpw......................................... 141 MUTU 27 ntch......................................... 145 MUTU 28 nkhw........................................ 148 MUTU 29 mphw....................................... 152 MUTU 30 Kubwereza............................... 155 MUTU 31 mtch........................................ 158 MUTU 32 nthw........................................ 162 MUTU 33 mtsw........................................ 166 MUTU 34 mnkhw..................................... 170 MUTU 35 Kubwereza............................... 174

MUTU 1 Malonje akusukulu bwanji kambirana

bwino buku

Ana okonda sukulu

Malita ndi Yohane adakumana pa tsiku lotsekulira sukulu. Iwo adakambirana za maphunziro awo motere. Yohane : Uli bwanji Malita?

Malita : Ndili bwino, kaya iwe? 1

Yohane : Kodi mu Sitandade 1, mabuku owonjezera udawerengapo? Malita : Eee, ndidawerenga.

Yohane : Nanenso ndidawerengapo. Mabukuwo adali osangalatsa. Malita : Ndikhulupirira mu Sitandade 2, tikhalanso ndi mabuku ena owonjezera. Yohane : Zikatero zikhala bwino. Malita : Tiye tikalowe m’kalasi. Yohane : Tiye, Malita.

Malita ndi Yohane adali okonzeka kuwerenga mabuku owonjezera a mu Sitandade 2.

2

Ntchito

A Mafunso

1 K  odi Malita ndi Yohane adakumana kuti? 2 M  alita ndi Yohane adakambirana za chiyani? 3 K  odi Malita ndi Yohane adasonyeza bwanji kuti ankakonda sukulu? B Kupanga ziganizo

Pangani ziganizo zomveka bwino ndi mawu awa: bwino

werenga



kambirana

kalasi

Chitsanzo

Petulo akuwerenga buku.

3

4

5

6

aA

ana

nN

nanazi

iI

insa

mM

mango

uU

uta 7

kK

kalulu

oO

ovololo

lL

lalanje

eE

emvulopu

wW

wailesi 8

tT

tebulo

dD

diso

sS

sefa

pP

poto

nd

ndalama 9

ch

chule

yY

yala

bB

buku

zZ

zala

gG

galu 10

rR

lira

fF

fulu

hH

hamala

jJ

jombo

vV

vava 11

MUTU 2

nd ch

kwe mwi

nso mlu

bwa

nd nda ndo ndi ndu nde ndodo

ndalama

ndiwo

mitundu

12

ndowa

Dimba la a Ndelemani

A Ndelemani anyamula ndowa ziwiri. Iwo aika ndowa kundodo. Ndowazo ndi zamitundu yosiyana. A Ndelemani amathirira kabichi m’dimba mwawo. Alendo ambiri amachita chidwi ndi dimbali. A Ndelemani amapeza ndalama zochuluka akagulitsa kabichi wawo. 13

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi a Ndelemani anyamula chiyani? 2 K  odi a Ndelemani amapeza chiyani akagulitsa kabichi? 3 M  ukuganiza ndi chifukwa chiyani a Ndelemani amathirira kabichi wawo? B Kupanga mawu

Pangani mawu poika nd m’mipata. Chitsanzo ___olo ndolo 1 __owa 2 __ere 3 __iwo 4 __ani 5 __ulu 14

ndo

mba

le

thi

mu

ch che cho cha chu chi chala

chiswe

chimanga

chidole

15

chulu

Chiswe chiluma Chikondi

Chikondi ndi mwana wa a Chekani. Iye amakhala ku Chongoni. Tsiku lina Chikondi anapita pachulu kuti akatenge dongo. Iye amafuna kuumba chidole. Akutenga dongolo, chiswe chachikulu chinamuluma. Chiswecho chinaluma chala chake chaching’ono. Iye analira chifukwa cha ululu. 16

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi Chikondi ndi mwana wa yani? 2 Ndi chifukwa chiyani Chikondi anakatenga dongo? 3 Ndi chifukwa chiyani Chikondi anakatenga dongo la pachulu? B Kulemba mawu

Lembani mawu kuchokera mu mabokosi otsatirawa: Chitsanzo

cho

yo

che

la

Mawu: chola, cheyo chi na cho

swe

chu

la

cha

lu 17

MUTU 3

dz ph

chu ndi

ngo kwa

swe

dz dza dzi dzu dze dzo madzi

dzombe

dzinja

dzuwa

18

udzu

Tadala aona dzombe Inali nyengo yadzinja dzuwa litatuluka. Tadala ankapita kumjigo kukatunga madzi. Madziwo anali woti asambe popita kusukulu. Asanafike kumjigoko, Tadala anaona dzombe. Dzombe lambiri linatera mu udzu.

19

Tadala anabwerera kumudzi mofulumira. Iye anakauza makolo ake za dzombelo. Makolowo anapita kukatola dzombe. Iwo amakonda kudya dzombe.

Ntchito

A Mafunso 1 Kodi Tadala amakatunga madzi kuti? 2 Kodi Tadala anaona chiyani pokatunga madzi? 3 Mukuganiza ndi chifukwa chiyani Tadala anakauza makolo ake za dzombe?

20

B K  upeza mawu amene ali ndi dz

Tsekani mzere kunsi kwa mawu amene ali ndi dz. Chitsanzo

Iye akudya dzungu. Iye akudya dzungu.

1 Ana akuothera dzuwa. 2 Atate atola dzombe. 3 Mudzi uli pafupi ndi nyanja.

21

dya mbe

dzi nga

go

ph phi pha phu pho phe phika

phiri

phoso

phokoso

22

phazi

Mwana wokonda maphunziro Eliza amakhala mu dera la Phanga. Derali lili pafupi ndi phiri. Iye amaphunzira pa sukulu ya Phanga. Amavala nsapato zansalu. Nsapatozo ndi zolingana ndi phazi lake. Popita kusukulu, iye amatenga phoso. Phosoli amaphika ndi makolo ake. Eliza sachita phokoso pophunzira. Iye amakonda maphunziro a Chichewa, Chingerezi ndi masamu. Aphunzitsi amamukonda chifukwa ndi mwana womvera. 23

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi Eliza amaphunzira kuti? 2 Ndi chifukwa chiyani aphunzitsi amakonda Eliza? 3 Kodi muzichita chiyani kuti aphunzitsi azikukondani? B Kupanga mawu

Pangani mawu poika phi phe pha pho m’mipata. Chitsanzo __wa

phewa 1 __ so 2 __ la 3 __ ri 24

MUTU 4

mf

m’b

phu nda phi che

wo

mf mfa mfo mfi mfu mfe mfolo

mfumu

imfa

25

mfundo

Kulandira chimanga

Mfumu Chidothi idaitanitsa makolo omwe adachita nawo chitukuko cholambula msewu. Iyo idafuna kuti alandire chimanga. Mfumu idauza makolo onse kuti akhale pamfolo. Iyo simafuna kuti pakhale chisokonezo. Makolowo adasangalala ndi mfundo imeneyi. Chisokonezo chikhoza kubweretsa imfa. Kumwambowu kudali asirikali andodo. Iwo amakhazikitsa bata. 26

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi adaitanitsa makolo ndani? 2 Ndi chifukwa chiyani makolowo adaitanidwa? 3 Ndi chifukwa chiyani makolo adasangalala ndi mfundo yokhala pamfolo? B Kupeza mawu omwe ali ndi mf

Pezani mawu amene ali ndi mf m’ziganizo zotsatirazi. Chitsanzo

Mfumu yakhala pa mpando. Mfumu yakhala pa mpando.

1 Makolo ali pamfolo. 2 Mfumu inatenga ndodo. 3 Iye adanena mfundo yabwino. 27

kha dzo

chi mfu

nse

m’b m’be m’bu m’bo m’ba m’bi m’bobo

m’bale

m’bawa

m’bandakucha

28

m’busa

Jenifa ndi m’bale wake

Tsiku lina Jenifa ndi m’bale wake adali paulendo. Iwo ankapita kumalo wosungirako nyama. Bambo awo omwe ndi m’busa adawaperekeza. Iwo adanyamuka m’bandakucha. Atafika kumaloko adaona njoka ya m’bobo. Njokayo idali mu mtengo wa m’bawa. Iwo adaopa kufika pafupi ndi m’bawawo. Bambo awo adawauza kuti m’bobo ukaluma umapha. Jenifa ndi m’bale wake adayenda molambalala m’bawa uja. 29

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi Jenifa ndi m’bale wake ankapita kuti? 2 Njoka ya m’bobo idali kuti? 3 Mukanakhala inu, mukanatani mutaona m’bobo? B Kufananitsa mawu

Pezani mawu mu B ofanana ndi omwe ali mu A. Chitsanzo

A 1 m’bobo

B 2 m’bobo

A

B

1 m’bobo

1 m’bawa

2 m’bale

2 m’bobo

3 m’bandakucha

3 m’bale

4 m’bawa

4 m’bandakucha 30

MUTU 5 Kubwereza 1 T  chulani liwu loyamba lopezeka mu mayina a zinthu zomwe zili mu mabokosiwa. Chithunzi choyamba mutu 3

Chithunzi choyamba mutu 2

31

2 T  chulani maliwu a malembo kuchokera mu mabokosiwa.

dz

m’b

mf

ch

nd

ph

3 W  erengani maphatikizo otsatirawa. nda

phu

chi

cho

chu

nde

pha

m’bu

m’ba

dze

m’bo

ndi

phe

m’bi

cha

dza

32

4 Werengani mawu otsatirawa. ndalama

m’bebe

mudzi

chule

dzana

ndodo

mfumu

m’bobo

phunzira

chimfine m’banga phiri

phokoso

chala

dzulo

chipatala

ndulu

phika

chake

ndiwo

chatupa

ndolo

dzira

mfolo

5 Werengani nkhani yotsatirayi. Amanga nyumba m’tauni

Makolo a Yamikani adapeza ndalama. Iwo adagula malo m’tauni. Mfumu ya deralo idachitira umboni pogula malowo. Malowo adali pafupi ndi chipatala. Iwo adamanga nyumba pamalopo. Makolowo adabzala

33

mitengo ya m’bawa. Masiku ambiri ankamva phokoso kuchokera kuchipatala. Mafunso

1 Kodi nyumba ya makolo a Yamikani adaimanga kuti? 2 Ndani adachitira umboni pogula malo? 3 Mukuganiza ndi chifukwa chiyani makolo a Yamikani adagula malo m’tauni?

34

MUTU 6 phi

mph nth mfu

dzo mba

che

mph mpha mpho mphi mphu mphe mphuno

mphongo

mphiri

mphamba

35

mphaka

Chisomo ndi Mphatso

Chisomo ndi Mphatso amaphunzira pasukulu ya Mphako. Tsiku lina

36

akupita kusukulu anaona mphaka. Iwo anakambirana motere. Chisomo : Kodi wamuona mphaka?

Mphatso : Eee, ndamuona. Akuoneka wokongola ngati wanga. Chisomo : Uli ndi mphaka?

Mphatso : Eee, ndili naye wamphongo. Chisomo : Kodi amakonda kutani? Mphatso : Amakonda kugona pamphasa.

Chisomo : Mphakayo amadya chiyani?

Mphatso : Iye amadya mpheta, mphamba ndi mphemvu. Chisomo : Kodi amazigwira bwanji? Mphatso : Iye amazidumphira.

Chisomo : Kodi ndi wamphamvu?

Mphatso : Eee! Dzulo anagwira njoka ya mphiri. 37

Chisomo : Ndiye siinamulume?

Mphatso : Inamuluma pamphuno ndi pamphumi koma anaipha. Chisomo ndi Mphatso anafika kusukulu ndipo analowa m’kalasi.

Ntchito

A Mafunso 1 Ndani anali ndi mphaka wamphongo? 2 Kodi mphakayo anagwira njoka yanji? 3 Mukuganiza ndi chifukwa chiyani mphaka amakonda kugona pamphasa?

38

B Kufananitsa zithunzi ndi mayina Fananitsani zithunzi zotsatirazi ndi mayina ake pogwiritsa ntchito manambala. Chitsanzo

1

1



mphaka

mphamba

2

mphasa

3

mphaka

4

mphemvu

39

mwe ngo mpha dzu ndi

nth ntha nthe ntho nthu nthi

nthenda

nthudza

nthanda

nthiwatiwa

40

nthenga

Nthano ya nthiwatiwa

Agogo anga a Nthenda adatiuza nthano. Iwo adati padali munthu dzina lake Khama. Iye adapita kuthengo kuti akadye nthudza. Khama akuyenda, adaona chinthu chokongola. Chinthucho chidali nthenga ya nthiwatiwa. Khamayo adafunafuna nthiwatiwayo. Ataiona adafuna 41

kuigwira kuti akaiwete. Nthiwatiwa idachita mantha ndipo idathawa. Iye adaithamangitsa mpaka adatopa. Khama adabwerera kumudzi modandaula. Iye adalingalira za nthiwatiwa mpaka nthanda idaoneka. Khama adadziwa kuti kwacha.

Ntchito

A Mafunso 1 Tchulani dzina la agogo amene adafotokoza nthano. 2 Kodi Khama adathamangitsa chiyani kuthengoko? 3 Kodi mukadatani mukadaona kuti kwada?

42

B Kusankha mawu okhala ndi nth Sankhani mawu omwe ali ndi nth mu ziganizo zotsatirazi. Chitsanzo Nthiwatiwa imathamanga kwambiri. Nthiwatiwa imathamanga kwambiri. 1 Iye anatola nthenga kuthengo. 2 Nthanda ndi nyenyezi. 3 Nthudza zimakoma.

43

MUTU 7

tch mgw

dza nthu the cho gwi

tch tcha tchi tchu tche tcho tchetcha

tcheru

tchalitchi

tchena

44

matchona

Matchona a ku Joni

Kalekale anthu ena ankapita ku Joni. Iwo ankayenda ulendo wapansi. Nthawi zina kukawadera ankagona patchire. Anthuwo ankagona mwatcheru kuopa zilombo zolusa. Iwo ankatchetcha patchirepo asanagone.

45

Anthu ambiri ankakhalitsa ku Joni. Iwo ankasanduka matchona. Amene ankabwerako ankavala bwino. Iwo ankatchena ngati akupita ku ukwati. Ambiri ankatchuka chifukwa cha kutchenako.

Ntchito

A Mafunso 1 Kodi kalekale anthu ankapita kuti? 2 Kodi anthu ankagoneranji mwatcheru patchire? 3 Mukuganiza kuti ndi chifukwa chiyani anthu ankayenda pansi popita ku Joni?

46

B Kufananitsa ziganizo Sankhani ziganizo za mu B zomwe zikufanana ndi za mu A. Chitsanzo

A 1 ndi B 2 1 2 3 4

A I wo agona patchire. A  kupita kutchalitchi. Litchowa lasowa. S  ukuluyi ndi yotchuka.

47

1 2 3 4

B Litchowa lasowa. I wo agona patchire. S  ukuluyi ndi yotchuka. A  kupita kutchalitchi.

bwe ndu tcho mwa bwi

mgw mgwa mgwe mgwi

mgwere

mgwalangwa

mgwazo

mgwirizano

48

Kusamalira mitengo

M’mudzi mwa a Kalima muli mitengo yosiyanasiyana. Ina mwa mitengoyo ndi mgwalangwa, m’bawa ndi mvunguti. Anthu am’mudzimo amasamalira mitengoyo mwamgwirizano. Iwo sadula mitengoyi mwachisawawa. Chaka chilichonse anthuwo amakumba mgwere waukulu. 49

Anthu ena amakumba mgwere mwamgwazo. Mgwerewo umatchinga madzi osefukira kuti asagwetse mitengoyo.

Ntchito

A Mafunso 1 Tchulani mitengo yomwe amaisamalira m’mudzi mwa a Kalima. 2 Ndi chifukwa chiyani anthu amakumba mgwere? 3 Fotokozani ubwino wosamalira mitengo.

50

B Kutsiriza ziganizo Tsirizani ziganizo poika mawu awa: mgwere, mgwirizano, mgwazo ndi mgwalangwa mu mipata yoyenera. Chitsanzo Anthu akukumba _______. Anthu akukumba mgwere. 1 Mtengo wa ________ ndi wautali. 2 Iye amagwira ntchito mwa______. 3 M________ ndi wofunika m’kalasi.

51

MUTU 8

ng’w mch

mgwe mvu mba ngo tchi

ng'w ng'wi ng'wa ng'we nyang’wa

zing'wenyeng'wenye

ng’waa

kang’wing’wi

52

Madyerero aufumu

Tsiku lina mu dera la a Nyang’wa munali madyerero aufumu. Kunali magule osiyanasiyana monga gule wamkulu, chimtali ndi honala. Akang’wing’wi anali komweko. Mfumu Nyang’wa inanyang’wadi monga mwa dzina lake. Amayi ndi abambo ng’oma ndi zing’wenyeng’wenye mwaluso. 53

Aliyense anavina monyang’wa. Mudzi wonse wa Nyang’wa unali teketeke.

Ntchito

A Mafunso 1 Kodi madyerero aufumu anachitikira kuti? 2 Tchulani magule atatu omwe anthu anavina pa mwambowu. 3 Fotokozani kufunika kwa magule pa mwambo waufumu.

54

B Kupanga mawu Pangani mawu poika maphatikizo awa: ng’wa, ng’we ndi ng’wi mu mipata yoyenera. Chitsanzo

nya________ nyang’wa

1 kang’wi______ 2 monya_______ 3 zi____nyeng’wenye

55

mku mwe nga ng’wi ng’o

mch mcha mchi mchu mche mcho mchimwene

mcheni

mchewere

mchikumbe

56

mchere

Mchikumbe waphindu

Chisomo ali ndi mchimwene wake Kamchacha. Kamchacha amakhala ku Mchezi. Iye ndi mchikumbe. Kamchacha amalima mbewu zosiyanasiyana. Zina mwa mbewuzo ndi mchewere, mapira ndi chimanga. Iye amawetanso nsomba monga mcheni, chambo ndi milamba.

57

Mchewere ndi mapira amagulitsa. Chimanga amadya ndi banja lake. Kamchacha alinso ndi golosale. Amagulitsa mchere, shuga ndi sopo. Anthu ambiri amadzagula mchere m’golosalemo.

Ntchito

A Mafunso

1 Tchulani dzina la mchimwene wake wa Chisomo. 2 Kodi mchimwene wake wa Chisomo amaweta nsomba zamtundu wanji? 3 Mukuganiza kuti Kamchacha anachita chiyani kuti akhale ndi golosale? B Kupeza mawu omwe ali ndi mch Pezani mawu atatu omwe ali ndi mch kuchokera mu nkhani ya “Mchikumbe waphindu.” Chitsanzo mchimwene 58

MUTU 9

khw phw

mchi nso shu tsa bwe

khw khwa

khwi

khwe

khwakhwawe

khwima

khwasula

khwanya

59

khwekhwe

Khwakhwawe akodwa pa khwekhwe

Idali nthawi yadzinja. Chimanga chidali chisadakhwime. Ndiwo zamasamba zidali ponseponse. Chimwemwe adatopa ndi kudyera khwanya. Iye adauza atate ake kuti akufuna kukhwasula. Atate akewo adatchera khwekhwe. Chimwemwe adasangalala kuti akhwasula. 60

Tsiku lotsatira, atatewo adapita kokazonda khwekhwelo. Atafika, adaimba likhweru kuitana Chimwemwe. Iye adathamangira komwe adatchera khwekhwelo. Zachisoni, iwo adapeza khwakhwawe. Khwakhwawe ndi chibuluzi chachikulu. Atate adamuonjola khwakhwawe uja modandaula. Khwakhwaweyo adathawa.

Ntchito

A Mafunso 1 Ndani adatchera khwekhwe? 2 Kodi Chimwemwe adatopa ndikudyera chiyani? 3 Mukuganiza kuti ndi chifukwa chiyani atate adaonjola khwakhwawe modandaula?

61

B Kupanga mawu Pangani mawu poika khwa, khwe kapena khwi mu mipata yoyenera. Chitsanzo ____khwawe khwakhwawe 1 ___ nya 2 ___ ma 3 ___ khwe

62

khwa tche njo ndi su

phw phwa

phwi

phwetekere phwanyika

63

phwe

iphwa chithaphwi phweka

A Chiphwafu akonza njinga A Chiphwafu adali pa ulendo wochokera kumsika. Kumsikako adagula phwetekere ndi nyama. Ali panjira, tayala la njinga yawo lidaphwa. A Chiphwafu adakhotera pachithaphwi. Iwo adachotsa

64

chubu mutayala. Adapopa chubucho ndi kuchinyika pachithaphwipo. Iwo adafuna kuona pomwe padabooka. Atakonza adapitiriza ulendo wawo. Iwo adasangalala popeza phwetekere wawo sadaphwanyike.

Ntchito

A Mafunso 1 Kodi a Chiphwafu ankachokera kuti? 2 Kodi a Chiphwafu adasangalala chifukwa chiyani? 3 Ndi chifukwa chiyani a Chiphwafu sadavutike pokonza njinga yawo?

65

B Kukonza mawu olakwika Konzani mawu otsatirawa omwe alembedwa molakwika. Chitsanzo pwanya phwanya 1 pwiti 2 pwetekere 3 pwete

66

MUTU 10 Kubwereza 1 Tchulani liwu loyamba lopezeka mu mayina a zinthu zomwe zili mu mabokosiwa.

67

2 Tchulani maliwu a malembo kuchokera mu mabokosiwa. mph

nth

tch

mgw

ng’w

mch

khw

phw

3 Werengani maphatikizo otsatirawa. mpho nthe

tchu

mgwa

ng’wi mche

khwe

phwe

mphu mgwe

mcho

ng’wa

khwi

phwi

mchu

tcho

68

4 Werengani mawu otsatirawa. mphamba

nthiwatiwa

mphemvu

tcheru

mgwere

nyang’wa

mcheni

khwangwala

nthudza

tchire

kang’wing’wi

khwanya

mphaka

mchikumbe

mgwidyo

69

5 Werengani nkhani yotsatirayi.

Mphaka ndi khwakhwawe

Kalekale kudali mchikumbe wina dzina lake Kalulu. Iye adali ndi anyamata awiri, Mphaka ndi Khwakhwawe. Iwo ankalima mbewu monga mchewere, phwetekere ndi chimanga. Mchikumbeyo adali wotchuka mu deralo. Iye ankakonda Mphaka chifukwa ankalimbikira kulima. Mphaka adayamba kudya zakudya zabwino za mchikumbeyu. Khwakhwawe adamuthamangitsa chifukwa cha ulesi. Kuyambira pomwepo, Khwakhwawe amakhala kuphanga. Mafunso 1 Tchulani dzina la mchikumbe. 2 Kodi Mphaka ndi Khwakhwawe ankagwira ntchito yanji kwa mchikumbe? 3 Kodi mu nkhaniyi mwaphunziramo chiyani? 70

MUTU 11 m g

mm

mgwi mche mpha tchu cho

mg mgi mge mga mgo mgu mganda

mgaiwa

mgugu

mgonero

71

mgolo

Tsiku laukwati

Tsiku laukwati kwathu Ndi tsiku lachisangalalo zedi Amayi amakonzekera kwambiri Iwo amagayitsa mgaiwa Mgaiwa amaphikira thobwa Thobwalo amaliphika mu mgolo Tsiku laukwati kwathu Ndi tsiku lachisangalalo kwambiri Abambo amavina mganda Mganda ndi gule wosangalatsa Povina pamamveka mgugu Akavina amadya mgonero 72

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi pokonzekera tsiku laukwati amayi amatani? 2 Kodi thobwa la pa ukwati amaliphika mu chiyani? 3 Mukuganiza ndi chifukwa chiyani anthu amavina magule pa ukwati? B Kupanga mawu

Pangani mawu oyenera kuchokera mu mabokosi potsatira chitsanzo ichi. mgo

nda

mga

lo

Mawu: mgolo, mganda mgu di mgo

gu

mga

nero

mgo

iwa 73

mge mbo

mfu mgi

dza

mm mmo mme mmu mmi mma

mmodzi

mmera

mmene

mmemo

74

mmisiri

Mmisiri waluso

M’mudzi mwa a Pindani muli nyumba yokongola kwambiri. Nyumbayi adamanga ndi mmisiri wamkazi, mmisiri dzina lake anali Zione Patani. Mmisiriyu ankamanga mwamsanga ndi mwaluso.

75

Mmisiriyu ali ndi mwana mmodzi. Iye ndi mwana wake ankakondanso kulima. M’munda mwawo munkakhala mmera wobiriwira zedi.

Ntchito

A Mafunso 1 Tchulani mudzi womwe mmisiri wamkazi ankakhala. 2 Kodi mmisiriyu ankagwira ntchito yanji? 3 Kodi inu mumafuna kudzagwira ntchito yanji?

76

B Kulemba lembo lalikulu

Lembani lembo lalikulu koyambirira kwa ziganizo zotsatirazi. Chitsanzo

madalitso amakonda kulima. Madalitso amakonda kulima. 1 mmisiri wathu ndi waluso. 2 iye ali ndi mwana mmodzi. 3 tonse timakonda kulima.

77

MUTU 12 pw

sh

mgo mka mme nyu dzi

pw pwi pwa pwe zipwete

pweteka

pwepwete

pwatapwata

78

pwayi

Zipwete zokoma

Tamanda amakonda zipwete. Zipwete zimakoma kwambiri. Tsiku lina Tamanda ndi anzake analowa m’munda. Iwo amafuna zipwete. Akufuna zipwetezo, anaona pwayi. Pwayiyo anatera pa chipwete. Iwo sanaope. Mwamwayi, anapeza zipwete zambiri. 79

Iwo anabwerera kumudzi ali osangalala. Atangofika, mvula inayamba kugwa pwatapwata. Tamanda ndi anzake anayang’anizana naseka pwepwete chifukwa sananyowe.

Ntchito

A Mafunso 1 Kodi Tamanda ankakonda chiyani? 2 Ndi chifukwa chiyani Tamanda ndi anzake anaseka pwepwete? 3 Kodi chikanachitika ndi chiyani mvula ikanawapeza panjira anawo?

80

B Kufananitsa zithunzi ndi mayina Fananitsani zithunzi zotsatirazi ndi mayina ake pogwiritsa ntchito manambala. Chitsanzo

1 pwepwete

1 pwepwete

2 zipwete

3 pwayi

4 pweteka

81

pwa mvu nza dzi

nyo

sh sho

she

sha

shati

shuga

shasha

shisha

82

shu

shosha

shi

Banja la a Shawa

Shila ndi mwana wa a Shawa. A Shawa amakonza mawailesi ndi mafoni. Akapeza ndalama, a Shawa amagula shuga ndi buledi. Shila amakonda phala lothira shuga. Shuga amazunitsa phala. Shila akadya phala lothira shuga, amasewera osatopa mwamsanga.

83

Tsiku lina Shila ndi amayi ake anapita kumsika. Kumsikako anagula chitenje, diresi ndi shati. Shatiyo inali ya abambo. A Shawa anaikonda shatiyo.

Ntchito

A Mafunso 1 Kodi Shila ndi mwana wa yani? 2 Ndi chifukwa chiyani Shila amakonda phala lothira shuga? 3 Ndi chifukwa chiyani a Shawa anasangalala ndi shati? B Kupeza mawu omwe ali ndi sh

Pezani mawu omwe ali ndi sh kuchokera mu nkhani yomwe mwawerenga. Chitsanzo

Mawu: Shawa

84

MUTU 13 nje

zw msi

zy

sha

gu

yo

zw zwi zwe zwa zweta

zwee

chizwezwe

zizwa

85

zizwitsa

Kuipa kwa chamba

Tsiku lina Chisomo ndi Dalo anacheza ndi mphunzitsi wawo motere. Mphunzitsi : Kodi ana inu munamvera wailesi dzulo? Chisomo

: Ayi, kodi amakamba zotani?

Mphunzitsi : Amakamba zoti chamba chimachititsa chizwezwe. Dalo

: Chizwezwe? 86

Mphunzitsi : Ee, wozweta mutu amazizwitsa. Chisomo

: Amazizwitsa bwanji?

Dalo

: Kusuta chamba ndi koipa, eti?

Mphunzitsi : Amadya zotoleza kudzala.

Mphunzitsi : Ee. Pewani kusuta chamba kuti mupewe kuchita chizwezwe. Chisomo

: Tamva aphunzitsi. Kusuta chamba si kwabwino. Chisomo ndi Dalo anabwerera kunyumba atazindikira za kuipa kosuta chamba.

Ntchito

A Mafunso 1 Kodi mphunzitsi amacheza ndi yani? 2 Ndi chifukwa chiyani kusuta chamba kuli koipa? 3 Kodi inu mungatani mutaona anzanu akusuta chamba? 87

B K  ulemba mzere kunsi kwa zw m’mawu Lembani mzere kunsi kwa zw mu mawu omwe ali m’munsiwa. Chitsanzo zwee zwee 1 kuzweta 2 zizwitsa 3 chizwezwe

88

zwe

dzu

mva

zo

chi

zy zye

zyi

zyu

zya

zyoli

zyolika

zyolizyoli

kazyozyo

89

zyo

Chifundo m’kalasi

M’mudzi mwa a Kazyozyo mudali mnyamata dzina lake Chifundo. Iye ankaphunzira pa sukulu ya Maziko. Nthawi zambiri aphunzitsi akamuyandikira, iye ankangozyolika. Tsiku lina aphunzitsi ake adamuitanira pambali ndipo adayankhulana motere. Mphunzitsi : N’chifukwa chiyani umakhala zyolizyoli? Chifundo : Palibe aphunzitsi. Mphunzitsi : Chifundo usaope. Fotokoza vuto lako.

90

Chifundo

: Kungoti ndilibe cholembera.

Chifundo

: Zikomo aphunzitsi.

Mphunzitsi : Ukanandiuza. Kwaya cholembera ichi.

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi Chifundo ankachokera m’mudzi mwa yani? 2 Tchulani dzina la sukulu yomwe Chifundo ankaphunzirapo. 3 Kodi inu mungatani mutakhala kuti mulibe cholembera? B K  upanga mawu Pangani mawu poika zy m’mipata. Chitsanzo __oli zyoli 1 __olika 2 ka__ozyo 3 __oli__oli 91

MUTU 14 nkh zyo phu

tsi

ngw mwe

kwa

nkh nkhe nkho nkha nkhu nkhi nkhumba

nkhosa

nkhanga

nkhuli

92

Ziweto za a Nankhoma

A Nankhoma amakhala mu dera la Liwonde. Iwo amaweta nkhuku, nkhunda, nkhanga, nkhosa ndi nkhumba. Nkhuku zimayendera limodzi ndi nkhanga pokadya kudzala.

93

A Nankhoma amakazinga nyama ya nkhuku, nkhunda ndi nkhanga pafupipafupi. Iwo amachita izi chifukwa cha nkhuli. A Nankhoma amagulitsa nkhumba ndi nkhosa kuti apeze ndalama. Ndalamazo amalipirira ana sukulu.

Ntchito

A Mafunso

1 Tchulani ziweto ziwiri zomwe a Nankhoma amaweta. 2 Ndi chifukwa chiyani a Nankhoma amakazinga nyama pafupipafupi? 3 Kodi inu mutakhala mlimi, mungawete ziweto zanji?

94

B Kutsiriza ziganizo

Tsirizani ziganizo polemba mawu awa: nkhunda, nkhuli, nkhosa ndi nkhanga mu mipata yoyenera. Chitsanzo

Nyama ya _____ ndi yofewa kwambiri. Nyama ya nkhosa ndi yofewa kwambiri. 1 _____ imafanana ndi njiwa. 2 _____ ili ndi mawanga. 3 A Nankhoma ali ndi _____.

95

nkho

nga

zi

pe

ngw ngwe

ngwi

ngwa

ngwazi

nsungwi

chinangwa

ngwere

96

lu

Ngwazi ya masamu

Wanangwa amakhala mu mzinda wa Lilongwe. Iye ali ndi anzake awiri, Sangwani ndi Ulemu. Onsewa amaphunzira pa sukulu ya Ngwangwa. Pa Ngwangwa pali nsungwi zambiri. Wanangwa ndi anzake amatenga chinangwa akamapita kusukulu. Wanangwa ndi wanzeru. Iye ndi 97

ngwazi pa phunziro la masamu. Iye amaphunzitsa anzake masamu. Aphunzitsi anamkonzera ulendo wopita kunyanja. Iye anakaona mvuwu m’madzi ndi ngwere pamchenga.

Ntchito

A Mafunso

1 Tchulani mayina atatu a ophunzira a pa sukulu ya Ngwangwa. 2 Kodi Wanangwa amatenga chakudya chanji popita kusukulu? 3 Mukuganiza ndi chifukwa chiyani ophunzira amayenera kuthandizana mu kalasi?

98

B Kupanga ziganizo Pangani ziganizo ndi mawu awa: chinangwa, chingwe, ngwazi ndi nsungwi. Chitsanzo Chilenje ndi ngwazi ya Chichewa.

99

MUTU 15 Kubwereza 1 Tchulani liwu loyamba lopezeka mu mayina a zinthu zomwe zili mu mabokosiwa.

100

2 Tchulani maliwu a malembo omwe ali mu mabokosiwa. mg

sh

zw

mm

ngw

pw

zy

nkh

3 Werengani maphatikizo otsatirawa. mga

shu

zwi

mmo

zye

ngwi

pwa

zyo

nkha

ngwe

sha

mmi

pwe

mgu

zwee

nkho

101

4 Werengani mawu otsatirawa. pwayi

mmisiri shuga

chipwirikiti mgolo

nkhumba

ngwangwa zizwitsa

nkhuku

mmera zipwete

shati

zweta

mganda nkhosa

ngwazi

5 Werengani nkhani yotsatirayi. Chipwirikiti pa ukwati

Pamudzi pa a Ngwangwa padali madyerero aukwati. Kudali zakudya ndi zakumwa zosiyanasiyana. Kudali ndiwo monga nyama ya nkhuku, nkhosa ndi nkhanga. Ena adavina mganda. Shasha wina adaba poto wa nyama ya nkhuku. Iye adachoka pamalopo mozemba. Adangoti khonde zwee.

102

Mayi wina adazizwa ndi mayendedwe ake. Mayiyo adakuwa. Padali chipwirikiti. Abambo ena adamugwira. Atamufunsa, iye adangoti zyoli.

Ntchito Mafunso

1 Kodi madyerero adachitikira kuti? 2 Kodi pa ukwatiwu padali ndiwo zanji? 3 Fotokozani kuipa kwa kuba.

103

MUTU 16

mts

nkhu gwi zwe

zyo

mga

mts mtse mtsu mtsa mtso mtsi mtsuko

mtsinje

mtsutso

mtsitsi

104

mtsetse

Ana abwino Ana abwino

Likangolira beru, ngo! Aphunzitsi m’kalasi n’kuwatulutsa Liwiro wakunyumba layambika Akathandize makolo pakhomo

105

Ana abwino Mokondwera ayenda pa mtsetse Mtsuko pamutu, chigubu m’manja Ulendo wa ku mtsinje Ana abwino Pofika amayi awalandira madzi Mokondwera awiritsa m’chidebe Amwe aukhondo madzi

Ntchito

A Mafunso

1 Perekani ntchito imodzi yomwe ana amagwira. 2 Tchulani ziwiya zomwe zili mu ndakatuloyi. 3 Fotokozani njira ina yosamalira madzi kuti akhale aukhondo.

106

B Kutsiriza ziganizo Tsirizani ziganizo poika mawu awa: mtsuko, mtsinje, mtsetse ndi mtsikana m’mipata yoyenera. Chitsanzo

Maliya ndi ________ wanzeru. Maliya ndi mtsikana wanzeru. 1 Amayi asenza ______ popita kumadzi. 2 Njinga imathamanga pa ______. 3 Anyamata akusambira mu ______ .

107

MUTU 17 mtse

mbw nya

dzi

kho

nza

mbw mbwe mbwa mbwi mbwanda mbwadza

tambwali tumbwa

108

mbwita

Luka ambwita

Padali mnyamata wina dzina lake Luka. Iye ankakonda kuonjola nyama mu misampha ya anzake. Tsiku lina Luka adaona mbwadza. Iye adapeza kalulu atakodwa. Pamene ankafuna kumuonjola, msampha udaduka. Adalumpha kuti ambwandire kaluluyo. Mwatsoka

109

adambwita ndi kugwera pamsamphapo. Luka adavulala kwambiri. Kalulu adathawa. Mtedza wapamsamphapo udangoti mbwee. Mwini msampha adamupeza. Iye adamuyankhula motumbwa kuti wapeza polekera. Luka adakadyera mbwanda. Iye adati sadzabanso.

Ntchito

A Mafunso

1 Tchulani dzina la mnyamata mu nkhaniyi. 2 Ndi chifukwa chiyani kalulu adathawa? 3 Fotokozani kuipa kwa kuba.

110

B Ndagi/zilapi Perekani matanthauzo a ndagi/zilapi zotsatirazi. Chitsanzo

Bokosi langa lotsekula ndi chala.

Yankho

mtedza

1 Zungulira uku tikumane uku. 2 Chimunda uko pokolola n’kumanja. 3 Phiri lakwathu lokwera ndi ana omwe.

111

MUTU 18

ndw

mpha mbwi gwe nkhu njo

ndw ndwa

ndwi

kondwa

nkhandwe

tsindwi

chikondwerero

112

ndwe

Nkhandwe ilowa m’mudzi Tsiku lina nkhandwe idalowa m’mudzi mwa Gondwa. Iyo idaona nkhuku pakhonde. Nkhandweyi idaganiza kuti ikapha nkhukuyo pakhala chikondwerero.

Nkhandwe idalumphira nkhukuyo. Nkhuku ija idaulukira pa tsindwi la nyumba. Tsindwili lidali losasuka. 113

Nkhukuyo idagwera m’nyumba. Nkhandwe sidakondwe. Iyo idabwerera kutchire. Maganizo achikondwerero adathera pomwepo.

Ntchito

A Mafunso

1 Nkhandwe idalowa m’mudzi mwa yani? 2 Tchulani komwe nkhandwe idapita italephera kugwira nkhuku. 3 Mukuganiza kuti tsindwi la nyumba lidasasuka ndi chiyani?

114

B Kutsiriza ziganizo Tsirizani ziganizo poika mawu oyenera m’mipata kuchokera m’mikutiramawu. Chitsanzo

Atate adapita ku ________ (kondwa, chikondwerero). Atate adapita ku chikondwerero. 1 Nkhuku yaulukira pa _______ (tsindwi, nkhandwe). 2 Usiku kunali mphepo ya ________ panyanja (tsindwi, namondwe). 3 Nkhanga zidagwidwa ndi _________ (tsindwi, nkhandwe).

115

MUTU 19

thw

ndwe nkhu mphi kho pha

thw thwe thwa

thwi

kuthwa

thwanima

thwetsa

thwanithwani

116

Nyengo yadzinja

Inali nyengo yadzinja. Kumwamba kunali thwanithwani. Kuthwanimaku kunabweretsa chiyembekezo cha mvula. Mvula ikagwa, zamoyo zambiri zimasangalala. Ziphaniphani zimachita thwanithwani. Usiku wina Kondwani anaona ziphaniphani zili thwanithwani. Iye anachita chidwi ndi kuthwanimaku. Anayitana m’bale wake Mwayi. Mwayi anali chithwango mu banja la a Bengo. Iye atabwera, anachitanso 117

chidwi ndi kuthwanimako. Mwayi anati ziphaniphani zinalengedwa kuti zizithwanima.

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi m’bale wake wa Kondwani anali yani? 2 Tchulani dzina la tizilombo tomwe timathwanima. 3 Zamoyo zimasangalala bwanji mvula ikagwa? B Kupeza thw m’mawu Pezani thw mu mawu awa. Chitsanzo

thwetsa

thwetsa

1 thwika 2 kuthwa 3 thwanima 118

MUTU 20 Kubwereza 1 Tchulani liwu loyamba lopezeka mu mayina a zinthu kapena zochitika zomwe zili mu mabokosiwa.

2 Tchulani maliwu a malembo kuchokera mu mabokosiwa.

mts

thw

mbw

ndw

119

3 Werengani maphatikizo otsatirawa. mtsa thwi mtsu ndwi ndwe mbwi thwa mbwe 4 Werengani mawu otsatirawa. mtsuko

mbwanda

kondwa

thwanima nkhandwe

mtsetse

mbwita

mtsitsi

thwika

tsindwi

kuthwa

chikondwerero

mbwee

thwanithwani ithwa

5 Werengani nkhani yotsatirayi. Mtsikana wolimba mtima

Gogo Mbwanda adali ndi mdzukulu wawo. Dzina lake lidali Takondwa. Gogoyu adapatsa Takondwa mtsuko. Iye adakondwera nawo mtsukowo. Takondwa adali mtsikana wolimba mtima. Tsiku lina adapita ku mtsinje kukatunga 120

madzi. Iye adatenganso chikwanje chakuthwa kuti akadulire nzimbe. Panjira Takondwa adaona nkhandwe. Nkhandweyo idamuopseza. Iye adatula pansi mtsukowo. Adaponya chikwanje kuti adziteteze. Iye adambwita. Mwamwayi nkhandweyo idathawa.

Ntchito Mafunso

1 Kodi mdzukulu wa Gogo Mbwanda adali yani? 2 Tchulani nyama yomwe mdzukulu wa Gogoyu adakumana nayo panjira. 3 Mukuganiza chikadachitika ndi chiyani Takondwa akadapanda kuponya chikwanje?

121

MUTU 21

thy

mbwa nji ndwe wo mtsu

thy thyo thyu thyi thya thye thyakula

thyola

thyakuka

thyoka

122

thyuka

Yohane aphika nsima

Amayi adauza Yohane kuti aphike nsima. Iye adali asadaphikepo. Yohane adathyola nkhuni zoti aphikire nsimayo. Asadayambe kuphika adakambirana ndi amayi ake motere. Amayi

: Yohane uphike nsima.

Yohane : Chabwino amayi, ndiphika. 123

Amayi

: Uphiketu nsima yothyakuka.

Amayi

: Usamale pothyakula kuti mthiko usathyoke.

Yohane : Inde amayi ndiyesetsa kuthyakula.

Yohane : Chabwino amayi. Yohane adaphika nsima. Banja lonse lidakondwera litadya nsima yothyakuka.

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi amayi adauza Yohane kuti aphike chiyani? 2 Ndi chifukwa chiyani banja lonse lidakondwera? 3 Mukuganiza kuti ndi bwino kuti anyamata aziphika?

124

B Mawu otsutsana m’matanthauzo Pezani mawu mu B otsutsana m’matanthauzo ndi omwe ali mu A. Chitsanzo A



B

A



B

pita

bwera

inde

abambo

amayi

kwiya

kondwa

bwera

pita

ayi

125

MUTU 22

tsw

thyo nsi ntha ndwe phu

tsw tswe tswere

tswi

tswa

katswiri

tswayitswayi

126

Thandizo apita kosaka

Thandizo adali wokonda kudya zatswayitswayi. Iye adali katswiri pa uzimba. Thandizo sankaphonya polasa nyama. Tsiku lina iye adapita kuphiri kukasaka nyama. Akusaka adaona udzu ukugwedera. Thandizo adayenda monyang’ama. 127

Atapenyetsetsa adaona kalulu. Iye adaponya chibonga. Kalulu adachiona chibongacho. Iye adangoti tswere patchire. Thandizo adadziwa kuti sakadyera zatswayitswayi.

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi Thandizo amakonda kudya zotani? 2 Kodi Thandizo ataona udzu ukugwedera adayenda motani? 3 Mukuganiza kuti kuipa kopha nyama zam’tchire mwachisawawa ndi kotani?

128

B Kupanga mawu Pangani mawu kuchokera ku malembo omwe ali mu mabokosiwa. Chitsanzo

yitswa tswayi

1

2

3

tswayitswayi

k a r i t s w i

________

l u k a l u

________

r e t s w e

________ 129

MUTU 23 ngo

msw tswe

ng’a

dzu

msw mswe mswachi

mswa mswera

mswankhono

130

mswi

phi

Kusamalira mano

Dzulo aphunzitsi anatiphunzitsa kasamalidwe ka mano. Anafotokoza kuti tizitsuka mano athu ndi mswachi. Iwo anati titha kugula mswachi kusitolo. Tithanso kupanga mswachi kuchokera ku kamtengo. Anatiphunzitsanso momwe tingapangire mswachi.

131

Patsikuli kunali mswera. Nditaweruka kusukulu, ndinakafuna kamtengo kokonzera mswachi. Ndili komweko ndinaona mbalame ya mswankhono. Mbalameyi imadya nkhono. Ndinachita mantha ndi mbalameyi komabe ndinadula kamtengoko.

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi ophunzira anaphunzira chiyani kusukulu? 2 Kodi mbalame ya mswankhono imadya chiyani? 3 Fotokozani ubwino wosamalira mano. B Kupanga mawu Pangani mawu okhala ndi msw, tsw, nkh. Chitsanzo nkh

nkhono 132

MUTU 24

nsw

tsa mswe nkho nzi thu

nsw nswa

nswe

nswi

nswala

inswa

nswachulu

133

Ulemu athawa nswala

Tsiku lina Ulemu adapita komwe kudali chulu. Iye ankafuna kukagwira inswa. Atayandikira chulucho, adaona nyama yodabwitsa. Nyamayo inkadya masamba a mtengo wa nswachulu. Iye adathawa. 134

Ulemu adafotokozera Mayi Nswati za nyamayo. Amayiwo adati nyamayo ndi nswala. Nswala imadya masamba akunsonga zamtengo. Chifukwa cha ichi, dzina lina la nswala ndi kadyam’nsonga.

Ntchito

A Mafunso

1 Ndi chifukwa chiyani Ulemu adapita komwe kudali chulu? 2 Kodi Ulemu adaona nyama yanji? 3 Kodi inu mutaona nyama yachilendo mungatani?

135

B Kutsiriza ziganizo Tsirizani ziganizo poika nswala, Nswati, inswa kapena nswachulu m’mipata yoyenera. Chitsanzo

Ulemu adaona Mayi _____. Ulemu adaona Mayi Nswati. 1 ________ ili ndi khosi lalitali. 2 Pachulu pamatuluka _______. 3 ________ ndi dzina la mtengo.

136

MUTU 25 Kubwereza 1 Tchulani liwu loyamba lopezeka mu mayina a zinthu kapena zochitika zomwe zili mu mabokosiwa.

2 Tchulani maliwu a malembo kuchokera mu mabokosiwa.

thy

tsw



msw

nsw

137

3 Werengani maphatikizo otsatirawa. thya nswi tswe mswi mswe thyi tswa thye tswe thyo mswa nswe nswa thya tswi thyu 4 W  erengani mawu otsatirawa. thyoka

nswachulu

tswere

tswii

katswiri

kathyali

mswachi

mswera

nswala

thyakula

mswankhono thyathyathya

inswa

thyapa

thyola

138

5 Werengani nkhani yotsatirayi.

A Thyolani apita kusitolo

A Thyolani adapita kusitolo yaikulu. Sitoloyi idali mu mzinda wa Mzuzu. Mwana wawo adawapempha kuti akamugulire mswachi. Mswachi wake udathyoka. Akazi awo adawauza kuti akagule ndiwo zatswayitswayi. A Thyolani atafika kusitoloko adagula mswachi ndi zipatso. Atafika pogulitsira nyama, adapeza nyama yoduladula ndi yogaya. A Thyolani adagula nyama yogaya. Atatuluka panja, adagulanso inswa. Kusitoloko adabwera dzuwa lili tswii.

139

Ntchito Mafunso

1 Kodi a Thyolani adapita kuti? 2 Tchulani zinthu zomwe a Thyolani adagula. 3 Mukuganiza chikadachitika ndi chiyani a Thyolani akadapanda kugula ndiwo?

140

MUTU 26

mpw

thyo tswi nswa chu bwe

mpw mpwa

mpwi

mpweya

141

mpwe

Mpweya Ine ndine mpweya Sindioneka kapena kugwirika Zamoyo ndi zopanda moyo zimandifuna Palibe opambana ine Ine ndine mpweya Zamoyo zimandifuna 142

Anthu, nyama ndi zomera zimandidalira Palibe opambana ine Ine ndine mpweya Kundisamalira ndimathandiza Bzalani mitengo kuti musangalale nane Pakuti palibe opambana ine.

Ntchito

A Mafunso

1 Ndani akuyankhula m’ndakatuloyi? 2 Tchulani zinthu zimene zimafuna mpweya. 3 Mukuganiza chingachitike ndi chiyani mpweya utasowa?

143

B K  usiyanitsa zinthu zofuna mpweya ndi zosafuna mpweya Lembani inde ngati chinthucho chimafuna mpweya kapena ayi ngati sichifuna mpweya. Chitsanzo nswala



___

nswala

inde

1 mwala

____

2 nthiwatiwa

____

3 inswa

____

144

MUTU 27

ntch

dwe tswi mpwa nthu nso

ntch ntcha ntchu

ntche ntcho

ntchi

ntchito

ntchofu

ntchentche

ntchafu

145

Linda asirira unamwino

Linda amakhala ndi atsibweni ake a Mwale. Atsibweni akewo amagwira ntchito ya unamwino. A Mwale amagwira ntchitoyo pa chipatala cha Ntcheu. Iwo amasamalira anthu odwala matenda osiyanasiyana. Matendawa ndi monga ntchofu, edzi, kamwazi ndi malungo. 146

A Mwale amaphunzitsanso za ukhondo. Iwo amati ntchentche zimafalitsa matenda. Ntchentche zimakonda zinthu zoola. Ntchentche sizifalitsa matenda ena monga ntchofu. Linda amasirira ntchito ya unamwino.

Ntchito

A Mafunso

1 Tchulani dzina la atsibweni a Linda. 2 Kodi Linda amasirira ntchito yanji? 3 Tchulani ntchito zomwe mumasirira ndi zifukwa zake? B Kuchita sewero Chitani sewero la malonje akuchipatala pakati pa namwino ndi wodwala.

147

MUTU 28

nkhw

mwa bwe kho ntchi phu

nkhw nkhwa

nkhwi

nkhwe

nkhwenzule

nkhwazi

nkhwangwa

nkhwidzi

148

nkhwiko

Nkhwenzule yankhwidzi

Kalekale, nkhwali, nkhwazi ndi nkhwenzule zinkakhalira limodzi. Nkhwazi idali mfumu. Mbalame zonsezi zinkakhala modalirana. Patapita nthawi, nkhwenzule idayamba nkhwidzi. Tsiku lina nkhwenzule idasowetsa nkhwangwa ya nkhwali mwadala. 149

Iyo idachita izi chifukwa cha khalidwe lake. Nkhwenzule sinkakondwa ndi kupeza bwino kwa nkhwali. Poopa mlandu, nkhwenzule idathawa. Kuyambira pomwepo, nkhwenzule imapezeka usiku wokhawokha.

Ntchito

A Mafunso

1 Tchulani mayina a mbalame zitatu mu nkhaniyi. 2 Ndi chifukwa chiyani mbalame ina idasowetsa nkhwangwa? 3 Mukuganiza kuti kuipa kwa nkhwidzi ndi kotani?

150

B Ndagi/zilapi Perekani matanthauzo a ndagi/zilapi zotsatirazi. Chitsanzo

Alira atadzimenya yekha. Yankho

tambala 1 Nyumba yanga yopanda khomo. 2 Ndili ndi mphasa koma ndimagona pansi. 3 Kankhalamba aka kugwaigwa.

151

MUTU 29 ngwa

mphw dwe

wo

nzu

nkhwi

mphw mphwe

mphwa

mphwephwa

mphwi

mphwayi

mphwene

152

Mphwayi A Nyoni ankakhala m’mudzi mwa Chitumphwa. Iwo adali amphwayi ndipo ankachita zinthu mwaulesi ndi mochedwa. Nthawi zambiri, akazi awo ankachita kuwadzutsa popita kumunda. A Nyoni akadzuka, amasukusula kuchotsa mphwene. 153

Akafika kumunda, ankalima mwamphwayi. Ankabzala ndikupalira mochedwa. Banja la a Nyoni linkakolola mphwephwa zokhazokha.

Ntchito

A Mafunso

1 Tchulani dzina la munthu wamphwayi mu nkhaniyi. 2 Ndi chifukwa chiyani banja la a Nyoni linkakolola mphwephwa zokhazokha? 3 Fotokozani kuipa kwa mphwayi. B Kupanga ziganizo

Pangani ziganizo ndi mawu awa: mphwayi, mphwephwa, mwaulesi ndi palira. Chitsanzo Tamandani amalima mwaulesi.

154

MUTU 30 Kubwereza 1 Tchulani liwu loyamba lopezeka mu mayina a zinthu kapena zochitika zomwe zili mu mabokosiwa.

2 Tchulani maliwu a malembo kuchokera mu mabokosiwa.

nkhw

mphw



mpw

ntch 155

3 Werengani maphatikizo otsatirawa. mphwa

nkhwe

ntchi

nkhwa

mpwe

mphwe

ntcho

nkhwi

mpwa

ntchu

mpwi

ntcha

4 Werengani mawu otsatirawa. nkhwangwa ntchuwa

mpweya

nkhwali

mphwephwa nkhwiko

nkhwesa

ntchofu

mphwene

nkhwazi

ntchafu

nkhwidzi

ntchentche mpweche mphwayi

nkhwere

nkhwenzule ntchito

156

5 Werengani ndakatulo yotsatirayi. Mlenje wankhuli

Onani mlenje wankhuli Iye sanyambitira mphwene Amalawirira kutchire kukasaka Kukasaka nkhwali ndi nkhanga Iye samasaka nkhwenzule ndi nkhwazi Onani mlenje wankhuli Iye sachita mphwayi posaka Posaka nyama m’nkhalango Amasaka ntchefu ndi mbawala Zankhuli zili mpweche m’nyumba mwake

Ntchito

Mafunso 1 Kodi mlenje amapita nthawi yanji kokasaka? 2 Tchulani mbalame zomwe mlenje amasaka. 3 Mukuganiza ndi chifukwa chiyani mlenje samasaka nkhwenzule ndi nkhwazi? 157

MUTU 31 mphwe

mtch nkha

tchi

nkhu

mtch mtcha mtche

mtchu mtchi

mtcho

mtchetcha

mtchona

mtchini

mtchatho

158

ngo

Matenda a mtchetcha

Upile amaphunzira pa sukulu ya Mtchanga. Abambo ake a Lomba adali mtchona. Iwo adakatchona ku dziko lakutali. Atabwerera kumudzi, adagula mtchini. Banja la a Lomba lidapindula ndi mtchiniwo. Tsiku lina, Upile ankacheza ndi abambo ake. Iye adawauza za 159

matenda omwe adaphunzira kusukulu. Matendawa amatchedwa mtchetcha. Iye adawauza bambowo kuti adafunsa mafunso ambiri. Upile adaphunzira kuti mtchetcha ndi matenda woopsa.

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi a Lomba adagula chiyani atabwerera kumudzi? 2 Kodi Upile adaphunzira zamatenda anji? 3 Mukuganiza ndi chifukwa chiyani a Lomba adakatchona ku dziko lakutali?

160

B Kulemba lembo lalikulu

Lembani lembo lalikulu koyambira kwa chiganizo chilichonse mu ziganizo zotsatirazi. Chitsanzo

mayamiko wagula mtchini. Mayamiko wagula mtchini. 1 mtchetcha ndi matenda oopsa. 2 amayi apita ku mtchini. 3 galimoto iyi ndi ya a Mtchona.

161

MUTU 32

nthw

psa mtche

dwi

tcho

thu

nthw nthwa

thanthwe

nthwe

nthwi

phunthwa

162

Nkhalango ya Liwonde

Tsiku lina Moyenda ndi Towera ankacheza motere. Towera : Iwe Moyenda, dzulo unali kuti? Moyenda : Ndinapita ku nkhalango ya Liwonde ndi makolo anga. Towera : Munakachita chiyani? 163

Moyenda : Kukaona nyama. Ee, koma ndinaphunthwa. Towera : Kuphunthwa? Iwe sumaona? Moyenda : Ndimachita mantha ndi mikango yomwe inali pathanthwe.

Towera : Imatani pathanthwepo?

Moyenda : Akuti imafuna iziona nyama zili patali. Towera : Nyamazo imazionera pathanthwepo? Moyenda : Ee, akuti mikangoyo ikaona nyamazo imazizembera ndi kuzigwira. Towera : Ndidzapite nanenso kuti ndikaione. Moyenda : Udzapitedi. Koma uzikayenda bwino kuti usakaphunthwe.

164

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi Moyenda anapita ndi yani ku nkhalango ya Liwonde? 2 Ndi chifukwa chiyani mikango imagona pathanthwe? 3 Kodi anthu amaioperanji mikango? B Kupeza matanthauzo a mawu Pezani matanthauzo a mawu omwe ali mu A kuchokera mu B. Chitsanzo thanthwe chimwala chachikulu A B phunthwa y  enda mosafuna kuti wina akuone  nkhalango chimwala chachikulu thanthwe gunda kanthu ndi phazi mwadzidzidzi zembera dera la mitengo yambiri 165

MUTU 33 nkha

mtsw phu

nso

nthwe

mtsw mtswa

mtswi

mtswatswa

166

mtswe

gwi

Mbala zigwidwa

Pa sukulu ya Msangu padali mtsikana dzina lake Melifa. Tsiku lina Melifa akupita kusukulu adamva mtswatswa. Mtswatswawo unkamvekera mu nkhalango ya sukuluyo. Melifa adadabwa nawo mtswatswawo.

167

Iye adatola miyala ndi kuponya komwe kunkachokera mtswatswawo. Miyalayo idavumbulutsa mbala zomwe zimabisa mabuku patchire. Mtswatswa udapitirira pamene mbala zinkathawa. Melifa adakuwa. Aphunzitsi ndi ophunzira adakhamukira kumaloko. Iwo adathamangitsa mbalazo ndi kuzigwira. Mbalazo adakazipereka kupolisi. Aphunzitsi adayamikira Melifa.

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi Melifa ankaphunzira kuti? 2 Kodi mbala zidabisa chiyani patchire? 3 Fotokozani kuipa kwa kuba zipangizo zasukulu.

168

B K  usankha zinthu zochita mtswatswa ndi zosachita mtswatswa Ikani mawu awa galu, anthu, mbuzi, nyumba, mkango, nkhuku, msewu ndi mitambo m’magulu a zinthu zochita mtswatswa ndi zosachita mtswatswa

Chitsanzo Zochita mtswatswa Zosachita mtswatswa galu

nyumba

1



1

2



2

3



3

169

MUTU 34 mtswa

mnkhw gwi

mve

cho

mbu

mnkhw mnkhwa

mnkhwi

mnkhwani

170

mnkhwe

Malonda a mnkhwani

A Lungu ndi munthu wotchuka mu dera lathu. Iwo amagulitsa mnkhwani. A Lungu amapikula mnkhwaniwo ku msika waukulu. Iwo amayenda khomo ndi khomo kugulitsa mnkhwaniwo. Mnkhwani womwe a Lungu amagulitsa suwonongeka msanga. 171

Iwo amatengera mnkhwani mudengu. A Lungu amaphimbira mnkhwaniwo ndi masamba anthochi. Anthu ambiri amakonda kugula mnkhwani wa a Lungu. A Lungu amatchuka ndi dzina loti a Kamnkhwani. Anthu adawapatsa dzinali chifukwa cha malonda awo.

Ntchito

A Mafunso

1 Kodi a Lungu amagulitsa chiyani? 2 Ndi chifukwa chiyani a Lungu amatchedwa a Kamnkhwani? 3 Fotokozani kufunika kwa mnkhwani.

172

B Kupanga mawu

Pangani mawu okhoza kuchokera ku malembo omwe ali mu mabokosiwa. Chitsanzo ms k

a i

1

m kh

o o

2

dz m

a i

3

d ng

u e

msika

173

MUTU 35 Kubwereza 1 Tchulani liwu loyamba lopezeka mu mayina a zinthu kapena zochitika zomwe zili mu mabokosiwa.

2 Tchulani maliwu a malembo kuchokera mu mabokosiwa.

mtch

nthw



mtsw

mnkhw

174

3 Werengani maphatikizo otsatirawa. mtchu

mnkhwa

mtchi

mtswa nthwe

mnkhwe

mtcho

mnkhwi

mtswe

mtswi

mtche

nthwa

4 Werengani mawu otsatirawa. mtchetcha

thanthwe

mtswatswa mnkhwani mtchona

mtchini

phunthwa

mtchatho

5 Werengani nkhani yotsatirayi. Mayi Gunde agula mtchini

Mayi Gunde anakhala zaka zambiri ku Zimbabwe. Iwo anali mtchona. Nthawi yomwe ankabwerera kumudzi anagula

175

mtchini wogaya chimanga. Anaika mtchiniwu pafupi ndi msika woyandikana ndi thanthwe. Tsiku lina usiku, mlonda wa pa mtchini anamva mtswatswa. Mtswatswawu unkamvekera kudimba la mnkhwani. Dimbali linali pafupi ndi mtchiniwo. Atasuzumira anaona munthu. Iye anaganiza kuti anali wakuba ndipo anakuwa. Anthu anagwira munthuyo ndi kupita naye kupolisi.

Ntchito Mafunso

1 Kodi Mayi Gunde anakhala zaka zingati ku Zimbabwe? 2 Tchulani malo omwe Mayi Gunde anaika mtchini wawo. 3 Ndi chifukwa chiyani anthu anamuganizira munthuyo kuti anali wakuba? 176